Amos 1:9 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Zimene akunena Chauta ndi izi: “Chifukwa anthu a ku Tiro akunka nachimwirachimwira, sindileka kuŵalanga. Iwo adapereka mtundu wathunthu wa anthu ku Edomu, osasunga chipangano chaubale chija.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Atero Yehova, Chifukwa cha zolakwa zitatu za Tiro, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwake; popeza anapereka anthu onse kwa Edomu, osakumbukira pangano lachibale;
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Turo akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza iwo anagulitsa mtundu wathunthu ku ukapolo ku Edomu, osasunga pangano laubale lija,
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Atero Yehova, Cifukwa ca zolakwa zitatu za Turo, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwace; popeza anapereka anthu onse kwa Edomu, osakumbukila pangano lacibale;