Amos 2:9 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
“Komabe ndine amene ndidaononga Aamori pamene Aisraele ankafika, ngakhale iwo aja anali ataliatali ngati mikungudza, ngakhale anali amphamvu ngati mitengo ya thundu. Ndidaŵaonongeratu zipatso zao m'mwamba ndiponso mizu yao pansi.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Koma ndinaononga Ine pamaso pa Aamori, amene msinkhu wao unanga msinkhu wa mikungudza, nakhala nayo mphamvu ngati thundu; koma ndinaononga zipatso zao m'mwamba, ndi mizu yao pansi.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
“Ine ndinawononga Aamori pamaso pawo, ngakhale iwo anali anthu ataliatali ngati mikungudza ndiponso amphamvu ngati mitengo ya thundu. Ndinawononga zipatso zawo ndiponso mizu yawo.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Koma ndinaononga Ine pamaso pa Aamori, amene msinkhu wao unanga msinkhu wa mikungudza, nakhala nayo mphamvu ngati thundu; koma ndinaononga zipatso zao m'mwamba, ndi mizu yao pansi.