Amos 4:11 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
“Ndidaononga ena mwa inu, monga momwe ndidaonongera Sodomu ndi Gomora. Otsaliranu munali ngati zikuni zofumula pa moto. Komabe simudabwerere kwa Ine.” Akutero Chauta.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndinagubuduza ena mwa inu, monga umo Mulungu anagubuduzira Sodomu ndi Gomora; ndipo inu munali ngati muuni wofumulidwa kumoto; koma simunabwerera kudza kwa Ine, ati Yehova.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
“Ndinawononga ena mwa inu monga ndinawonongera Sodomu ndi Gomora. Inu munali ngati chikuni choyaka chimene chafumulidwa pa moto. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndinagubuduza ena mwa inu, monga umo Mulungu anagubuduzira Sodomu ndi Gomora; ndipo inu munali ngati muuni wofumulidwa kumoto; koma simunabwerera kudza kwa Ine, ati Yehova.