Amos 8:12 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Anthu azidzangoyenda uku ndi uku kuchoka ku nyanja ina kunka ku nyanja inanso, azidzangoti piringupiringu kuchoka chakumpoto kunka chakuvuma. Azidzafunafuna mau a Chauta, koma osaŵapeza.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo adzayendayenda peyupeyu kuyambira kunyanja kufikira kunyanja ndi kuyambira kumpoto kufikira kum'mawa; adzathamangathamanga kufunafuna mau a Yehova, koma osawapeza.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Anthu azidzangoyendayenda kuchoka ku nyanja ina kupita ku nyanja ina. Azidzangoyendayenda kuchoka kumpoto kupita kummawa, kufunafuna mawu a Yehova, koma sadzawapeza.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo adzayendayenda peyupeyu kuyambira kunyanja kufikira kunyanja ndi kuyambira kumpoto kufikira kum'mawa; adzathamangathamanga kufunafuna mau a Yehova, koma osawapeza.