Deuteronomy 34:9 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Tsono Yoswa, mwana wa Nuni, adadzazidwa ndi nzeru, chifukwa Mose adaamsanjika manja kuti aloŵe m'malo mwake. Aisraele adamvera Yoswa, ndi kutsata malamulo onse amene Chauta adaŵapatsa kudzera mwa Mose.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo Yoswa mwana wa Nuni anadzala ndi mzimu wanzeru; popeza Mose adamuikira manja ake; ndi ana a Israele anamvera iye, nachita monga Yehova adauza Mose.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Tsono Yoswa, mwana wa Nuni anadzazidwa ndi mzimu wanzeru chifukwa nʼkuti Mose atamusanjika manja. Choncho Aisraeli anamumvera ndipo anachita zomwe Yehova analamula Mose.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo Yoswa mwana wa Nuni anadzala ndi mzimu wanzeru; popeza Mose adamuikira manja ace; ndi ana a Israyeli anamvera iye, nacita monga Yehova adauza Mose.