Esther 1:12 — Compare Translations
3 translations compared side by side
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Koma Vasiti mkazi wamkuluyo anakana kudza pa mau a mfumu adamuuza adindowo; potero mfumu idapsa mtima ndithu, ndi mkwiyo wake unatentha m'kati mwake.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Koma antchito atapereka uthenga wa mfumu kwa mfumukazi, Vasiti anakana kubwera. Tsono mfumu inakwiya ndi kupsa mtima.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Koma Vasiti mkazi wamkuruyo anakana kudza pa mau a mfumu adamuuza adindowo; potero mfumu idapsa mtima ndithu, ndi mkwiyo wace unatentha m'kati mwace.