Ezekiel 12:16 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Koma ndidzasiyako oŵerengeka amene adzapulumuke ku nkhondo, njala, ndi mliri, kuti akafotokoze nkhani yonse ya zochita zao zonyansa pakati pa mitundu ya anthu kumene akupitako. Apo adzadziŵa kuti Ine ndine Chauta.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Koma ndidzawasiya owerengeka apulumuke lupanga, ndi njala, ndi mliri, kuti afotokoze zonyansa zao kwa amitundu kumene afikako; ndipo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Koma ndidzasiyako ena pangʼono amene adzapulumuke ku lupanga, njala ndi mliri, kuti akafotokoze ntchito zawo zonse zonyansa pakati pa anthu achilendo kumene akupitako. Pamenepo adzadziwa kuti ndine Yehova.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Koma ndidzawasiya owerengeka apulumuke lupanga, ndi njala, ndi mliri, kuti afotokoze zonyansa zao kwa amitundu kumene afikako; ndipo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.