Ezekiel 12:6 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Usenze katundu wako pa phewa, iwo akuwona, ndipo upite kunja ku mdima. Uphimbe kumaso kotero kuti sungathe kuwona pansi, chifukwa ndakusandutsa chizindikiro chochenjeza anthu a m'banja la Israele.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Pamaso pao uwasenze paphewa pako, ndi kuwatulutsa kuli mdima, nuphimbe nkhope yako kuti usapenye dziko; popeza ndakuika chizindikiro cha nyumba ya Israele.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Usenze katundu wako pa phewa iwo akuona, ndipo upite kunja ku mdima. Uphimbe nkhope yako kuti usaone pansi, pakuti ndakusandutsa iwe chizindikiro chochenjeza Aisraeli.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Pamaso pao uwasenze paphewa pako, ndi kuwaturutsa kuli mdima, nuphimbe nkhope yako kuti usapenye dziko; popeza ndakuika cizindikilo ca nyumba ya Israyeli.