Ezekiel 13:19 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Mwandichotsa ulemu pamaso pa anthu anga, chifukwa chofuna kulandira manja angapo a barele ndiponso zidutswa chabe za buledi. Mukupha anthu osayenera kufa, ndipo mukupulumutsa anthu osayenera kukhala moyo, pomanamiza anthu angaŵa amene amamva zabodza zanuzo.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo mundidetsa mwa anthu anga kulandirapo barele wodzala manja, ndi zidutsu za mkate, kuipha miyoyo yosayenera kufa, ndi kusunga miyoyo yosayenera kukhala ndi moyo, ndi kunena mabodza kwa anthu anga omvera bodza.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Ponamiza anthu anga amene amamva za mabodza anu, inu mwapha anthu amene sanayenera kufa ndipo mwasiya ndi moyo amene sanayenera kukhala ndi moyo.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo mundidetsa mwa anthu anga kulandirapo barele wodzala manja, ndi zidutsu za mkate, kuipha miyoyo yosayenera kufa, ndi kusunga miyoyo yosayenera kukhala ndi moyo, ndi kunena mabodza kwa anthu anga omvera bodza.