Ezekiel 22:12 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Mwa iwe muli ena olandira ziphuphu kuti aphe anzao. Ena amalandira chiwongoladzanja ndi kupezapo phindu pa zimene amakongoza, ena amaopsa anzao kuti apeze phindu. Onsewo andiiŵala Ine. Ndikutero Ine Ambuye Chauta.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Analandira mphotho mwa iwe kukhetsa mwazi, walandira phindu loonjezerapo, wanyengerera anansi ako ndi kuwazunza, ndipo wandiiwala Ine, ati Ambuye Yehova.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Mwa iwe muli anthu amene amalandira ziphuphu kuti aphe anzawo; ena amachita katapira ndi kupeza phindu loposera muyeso; enanso amapeza phindu mwachinyengo poopseza anzawo. Ndipo mwandiyiwala Ine, akutero Ambuye Yehova.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Analandira mphotho mwa iwe kukhetsa mwazi, walandira phindu loonjezerapo, wanyengerera anansi ako ndi kuwazunza, ndipo wandiiwala Ine, ati Ambuye Yehova.