Ezekiel 24:21 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
‘Uza Aisraele mau anga akuti, Ndidzaipitsa Nyumba yanga imene mwakhala mukuinyadira kwambiri. Mumakondwa kwambiri poiwona, ndipo mumaikonda ndi mtima wonse. Ana anu aamuna ndi aakazi amene mudaŵasiya m'mbuyo, adzaphedwa ndi lupanga.’
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Nena ndi nyumba ya Israele, Atero Ambuye Yehova, Taona, ndidzadetsa malo anga opatulika, ulemerero wa mphamvu yanu, chokonda m'maso mwanu, chimene moyo wanu ali nacho chifundo; ndipo ana anu aamuna ndi aakazi otsalira inu adzagwa ndi lupanga.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
‘Awuze Aisraeli kuti: Ine Ambuye Yehova ndikuti: ndidzayipitsa Nyumba yanga yopatulika, nyumba imene mwakhala mukuyinyadira. Mumakondwa kwambiri poyiona, ndipo mumayikonda ndi mtima onse. Ana aamuna ndi aakazi amene munawasiya mʼmbuyo adzaphedwa ndi lupanga.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Nena ndi nyumba ya Israyeli, Atero Ambuye Yehova, Taona, ndidzadetsa malo anga opatulika, ulemerero wa mphamvu yanu, cokonda m'maso mwanu, cimene moyo wanu ali naco cifundo; ndipo ana anu amuna ndi akazi otsalira inu adzagwa ndi lupanga.