Ezekiel 29:3 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Umuuze kuti Ine Ambuye Chauta ndikuti, “ ‘Ndikukuimba mlandu iwe Farao mfumu ya ku Ejipito, iwe ching'ona chogona m'mitsinje mwako. Wanena kuti, mtsinje wa Nailo ndi wako, udaulenga ndiwe.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
nena, uziti, Atero Ambuye Yehova, Taona nditsutsana nawe, Farao mfumu ya Aejipito, ng'ona yaikulu yakugona m'kati mwa mitsinje yake, imene ikuti, Mtsinje wanga ndi wangatu, ndadzipangira ndekha uwu.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Uyiwuze mfumuyo kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “ ‘Ndine mdani wako, iwe Farao mfumu ya Igupto, iwe ngʼona yayikulu yogona pakati pa mitsinje yako. Umanena kuti, ‘Mtsinje wa Nailo ndi wanga; ndinadzipangira ndekha.’
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
nena, uziti, Atero Ambuye Yehova, Taona nditsutsana nawe, Farao mfumu ya Aigupto, ng'ona yaikuru yakugona m'kati mwa mitsinje yace, imene ikuti, Mtsinje wanga ndi wangatu, ndadzipangira ndekha uwu.