Ezekiel 39:11 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
“Pa tsiku limenelo Gogi ndidzampatsa malo a manda oti amuikemo ku dziko la Israele, m'chigwa cha anthu apaulendo, kuvuma kwa Nyanja Yakufa. Chigwacho chidzatsekera njira anthu odzera kumeneko, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzaikidwa kumeneko, ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo kudzachitika tsiku ilo, ndidzapatsa Gogi manda m'Israele, chigwa cha opitawo kum'mawa kwa nyanja; ndipo lidzaletsa opitawo, ndipo adzaika komweko Gogi ndi unyinji wake wonse, nadzachitcha, Chigwa cha unyinji wa Gogi.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
“Pa tsiku limenelo ndidzamupatsa Gogi manda mu Israeli, mʼchigwa cha apaulendo, kummawa kwa Nyanja Yakufa. Mandawo adzatseka njira ya apaulendo, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzayikidwa kumeneko. Ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo kudzacitika tsiku ilo, ndidzapatsa Gogi manda m'Israyeli, cigwa ca opitawo kum'mawa kwa nyanja; ndipo lidzaletsa opitawo, ndipo adzaika komweko Gogi ndi unyinji wace wonse, nadzacicha, Cigwa ca unyinji wa Gogi.