Ezra 10:1 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Pamene Ezara ankapemphera ndi kulapa, alikulira ndipo atadzigwetsa pansi ku Nyumba ya Mulungu, chinamtindi cha anthu chidabwera kwa iye kudzasonkhana. Panali amuna, akazi ndi ana, kuchokera m'dziko lonse la Israele, ndipo ankalira koopsa.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Pakupemphera Ezara tsono, ndi kuwulula ndi kulira misozi, ndi kudzigwetsa pansi pakhomo pa nyumba ya Mulungu, udamsonkhanira mwa Israele msonkhano waukulu ndithu wa amuna, ndi akazi, ndi ana; popeza anthu analira kulira kwakukulu.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Pamene Ezara ankapemphera ndi kuvomereza tchimo lawo, akulira ndipo atadzigwetsa pansi ku Nyumba ya Mulungu, anthu ambiri anabwera kwa iye kudzasonkhana naye. Panali amuna, akazi ndi ana, kuchokera mʼdziko lonse la Israeli ndipo ankalira kwambiri.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Pakupemphera Ezara tsono, ndi kuulula ndi kulira misozi, ndi kudzigwetsa pansi pakhomo pa nyumba ya Mulungu, udamsonkhanira mwa Israyeli msonkhano waukuru ndithu wa amuna, ndi akazi, ndi ana; popeza anthu analira kulira, kwakukuru.