Ezra 10:2 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Tsono Sekaniya, mwana wa Yehiyele, wa fuko la Elamu, adauza Ezara kuti, “Ife takhala osakhulupirika kwa Mulungu wathu, ndipo takhala tikukwatira akazi achilendo a mitundu ya m'maiko akunoŵa. Koma ngakhale zili choncho, chikhulupiriro chilipobe pakati pa Aisraele.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Pamenepo Sekaniya mwana wa Yehiyele, mwana wina wa Elamu, anambwezera Ezara mau, nati, Talakwira Mulungu wathu, tadzitengera akazi achilendo a mitundu ya dzikoli; koma tsopano chimtsalira Israele chiyembekezo kunena za chinthu ichi.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Ndipo Sekaniya, mwana wa Yehieli, wa fuko la Elamu, anawuza Ezara kuti, “Ife takhala osakhulupirika kwa Mulungu wathu ndipo takhala tikukwatira akazi achilendo a mayiko akunowa. Koma ngakhale zili chomwechi, chikhulupiriro chilipobe pakati pa Aisraeli.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Pamenepo Sekaniya mwana wa Yehiyeli, mwana wina wa Elamu, anambwezera Ezara mau, nati, Talakwira Mulungu wathu, tadzitengera akazi acilendo a mitundu ya dzikoli; koma tsopano cimtsalira Israyeli ciyembekezo kunena za cinthu ici.