Ezra 4:3 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Koma Zerubabele, Yesuwa, ndi atsogoleri ena otsala a mabanja a m'dziko la Israele adaŵayankha kuti, “Sitikusoŵa chithandizo chanu pa ntchito iyi yomangira Nyumba Mulungu wathu. Koma ife tokha tidzammangira Nyumba Chauta, Mulungu wa Israele, monga mfumu Kirusi, mfumu ya ku Persiya, adatilamula.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Koma Zerubabele, ndi Yesuwa, ndi akulu otsala a nyumba za makolo a Israele, anati kwa iwo, Sikuyenera ndi inu ndi ife kumangira Mulungu wathu nyumba, koma ife tokha pamodzi tidzamangira Yehova Mulungu wa Israele, monga mfumu Kirusi mfumu ya Persiya watilamulira.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Koma Zerubabeli, Yesuwa ndi atsogoleri ena otsala a mabanja a Aisraeli anayankha kuti, “Inu simungatithandize kumangira Nyumba Yehova, Mulungu wathu. Tokha tidzamumangira Nyumba Yehova, Mulungu wa Aisraeli, monga mfumu Koresi, mfumu ya Perisiya inatilamulira.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Koma Zerubabele, ndi Yesuwa, ndi akuru otsala a nyumba za makolo a Israyeli, anati kwa iwo, Sikuyenera ndi inu ndi ife kumangira Mulungu wathu nyumba, koma ife tokha pamodzi tidzamangira Yehova Mulungu wa Israyeli, monga mfumu Koresi mfumu ya Perisiya watilamulira.