Ezra 8:21 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Ku mtsinje wa Ahavako, ndidalengeza kuti anthu onse asale zakudya, adzichepetse pamaso pa Mulungu wathu ndi kumpempha kuti atitsogolere ife ndi ana athu, ndiponso kuti ateteze katundu wathu pa ulendo wathu.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Pamenepo ndinalalikira chosala komweko kumtsinje wa Ahava, kuti tidzichepetse pamaso pa Mulungu wathu, kumfunsa ationetsere njira yolunjika ya kwa ife, ndi ang'ono athu, ndi chuma chathu chonse.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Ku mtsinje wa Ahava, ndinalengeza kuti anthu onse asale zakudya, adzichepetse pamaso pa Mulungu wathu ndi kupempha kuti atiyendetse bwino ife ndi ana athu, ndi kuteteza katundu wathu yense.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Pamenepo ndinalalikira cosala komweko ku mtsinje wa Ahava, kuti tidzicepetse pamaso pa Mulungu wathu, kumfunsa ationetsere njira yolunjika ya kwa ife, ndi ang'ono athu, ndi cuma cathu conse.