Galatians 4:14 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Ngakhale matendawo anali ngati mayeso kwa inu, komabe simudandinyoze kapena kunyansidwa nane. Kwenikweni mudandilandira ngati mngelo wa Mulungu, kapenanso ngati Khristu Yesu mwini.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
ndipo chija cha m'thupi langa chakukuyesani inu simunachipeputsa, kapena sichinakunyansirani, komatu munandilandira ine monga mngelo wa Mulungu, monga Khristu Yesu mwini.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Ngakhale kuti matendawo anali ngati mayesero kwa inu, simunandinyoze kapena kunyansidwa nane. Komatu inu munandilandira ngati kuti ndinali mngelo wa Mulungu, ngati kuti ndinali Khristu Yesu mwini.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
ndipo cija ca m'thupi langa cakukuyesani inu simunacipeputsa, kapena sicinakunyansirani, komatu munandilandira ine monga mngelo wa Mulungu, monga Kristu Yesu mwini.