Galatians 6:17 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Kuyambira tsopano asandivutenso munthu wina aliyense, pakuti zipsera zimene ine ndili nazo pa thupi langa, zikutsimikiza kuti ndine wakewake wa Yesu.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Kuyambira tsopano palibe munthu andivute, pakuti ndili nayo ine m'thupi mwanga mikwingwirima ya Yesu.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Pomaliza wina asandivutitse, pakuti mʼthupi mwanga muli zizindikiro za Yesu.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Kuyambira tsopano palibe munthu andibvute, pakuti ndiri nayo ine m'thupi mwanga mikwingwirima ya Yesu.