Genesis 24:48 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Kenaka ndinaŵerama, nkupembedza Chauta. Ndinatamanda Chauta, Mulungu wa mbuyanga Abrahamu, chifukwa cha kunditsogolera bwino kwambiri. Chauta wandifikitsa kwa mbale wake wa mbuyanga, kumene ndapezako mwana wake amene adzakhale mkazi wa mwana wa mbuyanga.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo ndinawerama mutu wanga ndi kulambira Yehova, ndi kumyamikira Yehova, Mulungu wa mbuyanga Abrahamu, amene ananditsogolera ine m'njira yakuona, kuti ndikamtengere mwana wamwamuna wake mwana wa mkazi wa mphwake wa mbuyanga.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
kenaka ndinawerama pansi ndi kupembedza Yehova. Ndipo ndinatamanda Yehova, Mulungu wa mbuye wanga Abrahamu, amene anandilondolera mokhulupirika njira yanga. Iye wandifikitsa kwa mʼbale wake kumene ndapezera mbeta mwana wa mbuye wanga.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo ndinawerama mutu wanga ndi kulambira Yehova, ndi kumyamikira Yehova, Mulungu wa mbuyanga Abrahamu, amene ananditsogolera ine m'njira yakuona, kuti ndikamtengere mwana wamwamuna wace mwana wamkazi wa mphwace wa mbuyanga.