Genesis 26:18 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Kumeneko adafukulanso zitsime zimene anthu adaakumba pa nthaŵi ya Abrahamu bambo wake. Atafa Abrahamuyo, Afilisti adaazikwirira zitsimezo. Isaki adazitcha zitsimezo maina omwewo amene bambo wake ankazitchula.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo Isaki anafukulanso zitsime za madzi, anazikumba masiku a Abrahamu atate wake; chifukwa kuti Afilisti anazitseka atafa Abrahamu: ndipo anazitcha maina monga maina omwe anazitcha atate wake.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Isake anafukulanso zitsime zija zimene zinakumbidwa mu nthawi ya abambo ake Abrahamu. Atamwalira Abrahamu, Afilisti anakwirira zitsimezi. Tsono anazitcha mayina omwewo amene abambo ake anazitcha.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo Isake anafukulanso zitsime za madzi, anazikumba masiku a Abrahamu atate wace; cifukwa kuti Afilisti anazitseka atafa Abrahamu: ndipo anazicha maina monga maina omwe anazicha atate wace.