Genesis 27:1 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Isaki atakalamba, adachita khungu, mwakuti sankatha kupenya. Tsono adatumiza mau kuti Esau mwana wake wamkulu abwere. Atabwera, Isaki adamuitana kuti, “Mwana wanga!” Iye adavomera kuti, “Ŵaŵa.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo panali atakalamba Isaki, ndi maso ake anali akhungu losaona nalo, anamuitana Esau mwana wake wamwamuna wamkulu, nati kwa iye, Mwana wanga; ndipo anati kwa iye, Ndine pano.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Isake atakalamba maso ake anachita khungu mwakuti sankatha kuona. Iye anayitana mwana wake wamkulu Esau nati kwa iye, “Mwana wanga.” Iye anayankha, “Ine abambo.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo panali atakalamba Isake, ndi maso ace anali a khungu losaona nalo, anamuitana Esau mwana wace wamwamuna wamkuru, nati kwa iye, Mwana wanga; ndipo anati kwa iye, Ndine pano.