Genesis 27:36 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Pamenepo Esau adati, “Kameneka nkachiŵiri kundichenjeretsa iye uja. Nchosadodometsa kuti dzina lake ndi Yakobe. Ukulu wanga wauchisamba adandilanda, ndipo tsopano wandilandanso madalitso anga. Kodi monga madalitsowo simudandisungireko ndi pang'ono pomwe?”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo iye anati, Kodi si ndicho chifukwa anamutcha dzina lake Yakobo? Kuti wandinyenga ine kawiri aka; analanda ukulu wanga ndipo taonani, tsopano walanda mdalitso wanga. Ndipo anati, Kodi simunandisungira ine mdalitso?
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Esau anati, “Kodi nʼchifukwa chake iyeyu dzina lake lili Yakobo eti? Aka nʼkachiwiri kundinyenga: Anatenga ukulu wanga, pano watenga madalitso anga!” Kenaka anafunsa, “Kodi simunandisungireko ena madalitsowo?”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo iye anati, Kodi si ndico cifukwa anamucha dzina lace Yakobo? kuti wandinyenga ine kawiri aka; analanda ukulu wanga ndipo taonani, tsopano walanda mdalitso wanga. Ndipo anati, Kodi smunandisungira ine mdalitso?