Genesis 42:7 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Yosefe ataŵaona abale akewo, adaŵazindikira, koma adangochita ngati sadaŵadziŵe. Adayamba kuŵalankhula mozaza, naŵafunsa kuti, “Kodi inu mukuchokera kuti?” Iwo adayankha kuti, “Tikuchokera ku Kanani, tadzagula chakudya kuno.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo Yosefe anaona abale ake, ndipo anazindikira iwo, koma anadziyesetsa kwa iwo ngati mlendo, nanena kwa iwo mwankhanza: ndipo anati kwa iwo, Mufuma kuti inu? Nati iwo, Ku dziko la Kanani kudzagula chakudya.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Yosefe atangowaona abale ake anawazindikira, koma ananamizira kukhala ngati mlendo nawayankhula mwaukali kuwafunsa kuti, “Mwachokera kuti?” Iwo anayankha, “Ku dziko la Kanaani, tikudzagula chakudya.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo Yosefe anaona abale ace, ndipo anazindikira iwo, koma anadziyesetsa kwa iwo ngati mlendo, nanena kwa iwo mwankhanza: ndipo anati kwa iwo, Mufuma kuti inu? nati iwo, Ku dziko la Kanani kudzagula cakudya.