Genesis 43:11 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Tsono bambo wao Israele adaŵauza kuti, “Ngati ndi m'mene ziliri, chitani choncho. Munthuyo mtengereniko zipatso zokoma za dziko lino m'matumba mwanu kuti mukampatse. Mumtengerenso mafuta opaka pang'ono, uchi pang'ono, mafuta onunkhira osiyanasiyana, mure, mtedza, ndiponso zipatso zinanso.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo Israele atate wao anati kwa iwo, Ngati chomwecho tsopano chitani ichi: tengani zipatso za m'dziko muno m'zotengera zanu, mumtengere munthu uja mphatso, mafuta amankhwala pang'ono, ndi uchi pang'ono, zonunkhira ndi mure, ndi mfula, ndi katungurume;
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Tsono abambo awo Israeli anawawuza kuti, “Ngati pafunika kutero, ndiye muchite izi: Ikanimo zipatso zabwino kwambiri za dziko lino mʼmatumba mwanu ndi kumutengera munthuyo ngati mphatso. Mumutengere mafuta wopaka pangʼono, uchi pangʼono, mafuta wonunkhiritsa chakudya, mule, mtedza ndi alimoni.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo Israyeli atate wao anati kwa iwo, Ngati comweco tsopano citani ici: tengani zipatso za m'dziko muno m'zotengera zanu, mumtengere munthu uja mphatso, mafuta a mankhwala pang'ono, ndi uci pang'ono, zonunkhira ndi mure, ndi mfula, ndi katungurume;