Habakkuk 2:5 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Monga munthu wokhuta vinyo ali wosokonezeka, chonchonso munthu wodzitama ndi wosakhazikika. Ndi waumbombo kwambiri ngati manda, ngati imfa amakhala wosakhuta. Amagwira anthu a mitundu yonse, amaŵasonkhanitsa ngati ake.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndiponso vinyo ngwonyenga, ngati munthu wodzikuza, wosakhala kwao; wakukulitsa chikhumbo chake ngati kunsi kwa manda, akunga imfa, yosakhuta, koma adzisonkhanitsira amitundu onse, nadzimemezera mitundu yonse ya anthu.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Ndithu, wasokonezeka ndi vinyo; ndi wodzitama ndiponso wosakhazikika. Pakuti ngodzikonda ngati manda, ngosakhutitsidwa ngati imfa, wadzisonkhanitsira mitundu yonse ya anthu ndipo wagwira ukapolo anthu a mitundu yonse.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndiponso vinyo ngwonyenga, ngati munthu wodzikuza, wosakhala kwao; wakukulitsa cikhumbo cace ngati kunsi kwa manda, akunga imfa, yosakhuta, koma adzisonkhanitsira amitundu onse, nadzimemezera mitundu yonse ya anthu.