Hebrews 9:7 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Koma m'chipinda chachiŵiri chija ndi mkulu wa ansembe onse yekha amene amaloŵamo, nayenso ndi kamodzi kokha pa chaka, ndipo saloŵamo popanda kutenga magazi. Magaziwo ngokapereka kwa Mulungu chifukwa cha iye mwini, ndiponso chifukwa cha machimo ochita anthu mosazindikira bwino.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
koma kulowa m'chachiwiri, mkulu wa ansembe yekha kamodzi pachaka, wosati wopanda mwazi, umene apereka chifukwa cha iye yekha, ndi zolakwa za anthu;
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Koma Mkulu wa ansembe yekha ndiye ankalowa chipinda chachiwiri chija kamodzi kokha pa chaka. Iye sankalowamo wopanda magazi. Magaziwo ankapereka nsembe kwa Mulungu chifukwa cha iye mwini ndiponso chifukwa cha machimo a anthu amene ankachita mosazindikira.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
koma kulowa m'caciwiri, mkuru wa ansembe yekha kamodzi pacaka, wosati wopanda mwazi, umene apereka cifukwa ca iye yekha, ndi zolakwa za anthu;