Hosea 12:1 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Efuremu chakudya chake ndi mpweya wokhawokha. Amanka nasaka mphepo yakuvuma tsiku lonse. Amachulukitsa mabodza ndi chiwawa. Amachita chipangano ndi dziko la Asiriya, ndipo amapereka mitulo ya mafuta ku Ejipito.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Efuremu akudya mphepo, natsata mphepo ya kum'mawa; tsiku lonse achulukitsa mabodza ndi chipasuko, ndipo achita pangano ndi Asiriya, natenga mafuta kunka nao ku Ejipito.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Efereimu amadya mpweya; tsiku lonse amasaka mphepo ya kummawa ndipo amachulukitsa mabodza ndi chiwawa. Amachita mgwirizano ndi Asiriya ndipo amatumiza mphatso za mafuta a olivi ku Igupto.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Efraimu akudya mphepo, natsata mphepo ya kum'mawa; tsiku lonse acurukitsa mabodza ndi cipasuko, ndipo acita pangano ndi Asuri, natenga mafuta kumka nao ku Aigupto,