Hosea 2:13 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Ndidzamlanga chifukwa choti adafukiza lubani kwa Abaala pa zikondwerero zao. Ankadzikongoletsa povala mphete ndi mikanda yamtengowapatali, kuti azithamangira zibwenzi zake, Ine nkumandiiŵala. Ndatero Ine Chauta.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo ndidzamlanga chifukwa cha masiku a Abaala amene anawafukizira, navala mphete za m'mphuno, ndi zokometsera zake, natsata omkonda, nandiiwala Ine, ati Yehova.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Ndidzamulanga chifukwa cha masiku amene anafukiza lubani kwa Abaala; anadzikongoletsa povala mphete ndi mikanda yamtengowapatali ndipo anathamangira zibwenzi zake, koma Ine anandiyiwala,” akutero Yehova.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo ndidzamlanga cifukwa ca masiku a Abaala amene anawafukizira, nabvala mphete za m'mphuno, ndi zokometsera zace, natsata omkonda, nandiiwala Ine, ati Yehova.