Hosea 6:3 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Tiyeni tilimbikire kusamala za Chauta. Adzabwera kwa ife mosapeneka konse ngati mbandakucha. Kubwera kwake kudzakhala madalitso ngati mvula, mvula yake yachilimwe imene imakhathamiza nthaka.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Tidziwe tsono, tilondole kudziwa Yehova; kutuluka kwake kwakonzekeratu ngati matanda kucha; ndipo adzatidzera ngati mvula, ngati mvula ya masika yakuthirira dziko.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Tiyeni timudziwe Yehova, tiyeni tilimbike kumudziwa Iye. Adzabwera kwa ife mosakayikira konse ngati kutuluka kwa dzuwa; adzabwera kwa ife ngati mvula ya mʼchilimwe, ngati mvula ya nthawi yamphukira imene imakhathamiritsa nthaka.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Tidziwe tsono, tilondole kudziwa Yehova; kuturuka kwace kwakonzekeratu ngati matanda kuca; ndipo adzatidzera ngati mvula, ngati mvula ya masika yakuthirira dziko.