Hosea 7:1 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Ndikati ndibwezere anthu anga pabwino, ndikati ndichiritse Aisraele, uchimo wao umaonekera poyera. Ntchito zoipa za anthu a ku Samariyawo sizibisika ai. Sakhulupirika, amanyenga anthu, amathyola nyumba ngati mbala, ndi achifwamba, amalandanso zinthu za anthu poyera.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
M'mene ndichiritsa Israele, mphulupulu ya Efuremu ivumbuluka, ndi zoipa za Samariya; pakuti achita bodza, ndipo mkhungu alowa m'nyumba, ndi gulu la mbala lilanda kubwalo.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Pamene ndichiritsa Israeli, machimo a Efereimu amaonekera poyera ndiponso milandu ya Samariya sibisika. Iwo amachita zachinyengo, mbala zimathyola nyumba, achifwamba amalanda anthu katundu mʼmisewu.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
M'mene ndiciritsa Israyeli, mphulupulu ya Efraimu ibvumbuluka, ndi zoipa za Samariya; pakuti acita bodza, ndipo mkhungu alowa m'nyumba, ndi gulu la mbala manca kubwalo.