Isaiah 31:1 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Tsoka kwa amene amapita ku Ejipito kukapempha chithandizo. Iwo amadalira akavalo, ndipo amakhulupirira kuchuluka kwa magaleta ao ankhondo, ndiponso mphamvu za asilikali ao okwera pa akavalo. Koma sakhulupirira Woyera uja wa Israele, kapena kupempha chithandizo kwa Chauta.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Tsoka kwa iwo amene atsikira kunka ku Ejipito kukathandizidwa, natama akavalo; nakhulupirira magaleta, pakuti ali ambiri, ndi okwera pa akavalo, pakuti ali a mphamvu zambiri; koma sayang'ana Woyera wa Israele, ngakhale kumfuna Yehova!
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Tsoka kwa amene amapita ku Igupto kukapempha chithandizo, amene amadalira akavalo, nakhulupirira kuchuluka kwa magaleta awo ankhondo ndiponso mphamvu za asilikali awo okwera pa akavalo, koma sakhulupirira Woyerayo wa Israeli, kapena kupempha chithandizo kwa Yehova.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Tsoka kwa iwo amene atsikira kunka ku Aigupto kukathandizidwa, natama akavalo; nakhulupirira magareta, pakuti ali ambiri, ndi okwera pa akavalo, pakuti ali a mphamvu zambiri; koma sayang'ana Woyera wa Israyeli, ngakhale kumfuna Yehova!