Isaiah 37:30 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Tsono Yesaya adauza mfumu Hezekiya kuti, “Chizindikiro cha zimene zidzachitika ndi ichi: Chaka chino mudzadya tirigu wa mphulumukwa. Chaka chamaŵa mudzadya tirigu wongodzimerera. Tsono chaka chamkucha mudzabzala tirigu ndi kukolola, mudzaoka mitengo yamphesa nkudya zipatso zake.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo ichi chidzakhala chizindikiro kwa iwe: chaka chino mudzadya zimene zili zomera zokha, ndipo chaka chachiwiri mankhokwe ake; ndipo chaka chachitatu bzalani ndi kudula ndi kulima minda yamphesa ndi kudya chipatso chake.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
“Iwe Hezekiya, chizindikiro chako cha zimene zidzachitike ndi ichi: “Chaka chino mudzadya zimene zamera zokha, ndipo chaka chachiwiri zimene zaphukira pa zomera zokha, koma chaka chachitatu mudzafesa ndi kukolola, mudzawoka mitengo yamphesa ndi kudya zipatso zake.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo ici cidzakhala cizindikilo kwa iwe: caka cino mudzadya zimene ziri zomera zokha, ndipo caka caciwiri mankhokwe ace; ndipo caka cacitatu bzalani ndi kudula ndi kulima minda yamphesa ndi kudya cipatso cace.