Isaiah 42:25 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Motero adatikwiyira kwambiri, nativutitsa ndi nkhondo. Adayatsa moto ponseponse potizungulira, ife osamvetsa. Moto udatipsereza, koma ife osapezapo phunziro ai.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Chifukwa chake anatsanulira pa iye mkwiyo wake waukali, ndi mphamvu za nkhondo; ndipo unamyatsira moto kuzungulira kwake, koma iye sanadziwe; ndipo unamtentha, koma iye sanachisunge m'mtima.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Motero anawakwiyira kwambiri, nawavutitsa ndi nkhondo. Anayatsa moto ponseponse mowazungulira komabe iwo sanamvetse; motowo unawapsereza, koma iwo sanatengepo phunziro ayi.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Cifukwa cace anatsanulira pa iye mkwiyo wace waukali, ndi mphamvu za nkhondo; ndipo unamyatsira moto kuzungulira kwace, koma iye sanadziwa; ndipo unamtentha, koma iye sanacisunga m'mtima.