Isaiah 44:9 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Onse amene amapanga mafano ngachabe, milungu imene amailemekeza kwambiri ndi yopanda phindu. Amene amaipembedza ndi akhungu ndi osadziŵa kanthu, choncho adzaŵachititsa manyazi.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Omwe apanga fano losema onsewo asokonezeka; ndipo zokondweretsa zao sadzapindula nazo kanthu; ndipo mboni zao siziona, kapena kudziwa; kuti akhale ndi manyazi.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Onse amene amapanga mafano ngachabe, ndipo milungu imene amayilemekeza ndi yopanda phindu. Iwo amene amapembedza mafano ndi wosaona; ndipo sazindikira kanthu. Choncho adzawachititsa manyazi.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Omwe apanga fano losema onsewo asokonezeka; ndipo zokondweretsa zao sadzapindula nazo kanthu; ndipo mboni zao siziona, kapena kudziwa; kuti akhale ndi manyazi.