Isaiah 47:14 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
“Taona, anthuwo ali ngati mapesi, adzapsa ndi moto. Sangathe kudzipulumutsa ku mphamvu ya malaŵi ake. Moto wake si woti nkuwotha kapena kusendera pafupi nawo ai.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Taona, iwo adzakhala ngati ziputu, moto udzawatentha iwo; sadzadzipulumutsa okha kumphamvu za malawi; motowo sudzakhala khala loothako, pena moto wakukhalako.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Ndithudi, anthuwo ali ngati phesi; adzapsa ndi moto. Sangathe kudzipulumutsa okha ku mphamvu ya malawi a moto. Awa si makala a moto woti wina nʼkuwotha; kapena moto woti wina nʼkuwukhalira pafupi.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Taona, iwo adzakhala ngati ziputu, moto udzawatentha iwo; sadzadzipulumutsa okha ku mphamvu za malawi; motowo sudzakhala khala loothako, pena moto wakukhalako.