Isaiah 48:20 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
“Tulukani m'dziko la Babiloni, thaŵani m'dziko la ukapolo. Mulengeze zimenezi ndi mau amphamvu, muzilalike, muzifikitse mpaka ku mathero a dziko lapansi. Muzinena kuti, ‘Chauta waombola Yakobe, mtumiki wake.’ ”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Tulukani inu m'Babiloni, athaweni Ababiloni; ndi mau akuimba nenani inu, bukitsani ichi, lalikirani ichi, ngakhale ku malekezero a dziko; nenani, Yehova waombola mtumiki wake Yakobo.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Tulukani mʼdziko la Babuloni! Thawani dziko la Kaldeya! Lengezani zimenezi ndi mawu a chisangalalo ndipo muzilalikire mpaka kumathero a dziko lapansi; muzinena kuti, “Yehova wawombola Yakobo mtumiki wake.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Turukani inu m'Babulo, athaweni Akasidi; ndi mau akuyimba nenani inu, bukitsani ici, lalikirani ici, ngakhale ku malekezero a dziko; nenani, Yehova waombola mtumiki wace Yakobo.