Isaiah 51:22 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Chauta, Ambuye ako, Mulungu wako, amene amakutchinjiriza, akunena kuti, “Ona, ndakulanda chikho chochititsa chizwezwe chija. Chikhocho, chimene ndidakupatsani ndili wokwiya, sudzachimwanso.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
atero Ambuye ako Yehova, ndi Mulungu wako amene anena mlandu wa anthu ake, Taona, ndachotsa m'dzanja mwako chikho chonjenjemeretsa, ngakhale mbale ya chikho cha ukali wanga; iwe sudzamwa icho kawirinso.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Ambuye Yehova wanu, Mulungu amene amateteza anthu ake akuti, “Taona, ndachotsa mʼdzanja lako chikho chimene chimakuchititsa kudzandira; sudzamwanso chikho cha ukali wanga.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
atero Ambuye ako Yehova, ndi Mulungu wako amene anena mlandu wa anthu ace, Taona, ndacotsa m'dzanja mwako cikho conjenjemeretsa, ngakhale mbale ya cikho ca ukali wanga; iwe sudzamwa ico kawirinso.