Isaiah 51:9 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Dzambatukani, Inu Chauta, dzambatukani! Valani dzilimbe. Dzambatukani monga momwe munkachitira masiku amakedzana, nthaŵi ya mibadwo yakale. Kodi sindinu uja mudaduladula Rahabu, chilombo cham'nyanja chija, ndi kubaya chinjoka cham'nyanja chija?
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Galamuka, galamuka, khala ndi mphamvu, mkono wa Yehova; galamuka monga masiku akale, mibadwo ya nthawi zakale. Kodi si ndiwe amene unadula Rahabu zipinjirizipinjiri; amene unapyoza chinjoka chamnyanja chija?
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Dzambatukani, dzambatukani! Valani zilimbe, Inu Yehova; dzambatukani, monga munkachitira masiku amakedzana, monga nthawi ya mibado yakale. Si ndinu kodi amene munaduladula Rahabe, amene munabaya chinjoka cha mʼnyanja chija?
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Galamuka, galamuka, khala ndi mphamvu, mkono wa Yehova; galamuka monga masiku akale, mibadwo ya nthawi zakale. Kodi si ndiwe amene unadula Rahabu zipinjiri zipinjiri, amene unapyoza cinjoka cija?