Isaiah 54:4 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
“Usaope, chifukwa sadzakunyozanso, usataye mtima poti sadzakupeputsanso. Udzaiŵala zimene zidakuchititsa manyazi pa unyamata wako, manyazi a pa umasiye wako sudzaŵakumbukanso.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Usaope, pakuti sudzakhala ndi manyazi; usasokonezedwe, pakuti sudzachitidwa manyazi; pakuti udzaiwala manyazi a ubwana wako, ndi chitonzo cha umasiye wako sudzachikumbukiranso.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
“Usachite mantha; sadzakunyozanso. Usakhumudwe; sudzapeputsidwanso. Udzayiwala za manyazi zimene zinakuchitikira nthawi ya unyamata wako ndipo za manyazi zimene zinakuchitikira pa nthawi ya umasiye wako sudzazikumbukanso.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Usaope, pakuti sudzakhala ndi manyazi; usasokonezedwe, pakuti sudzacitidwa manyazi; pakuti udzaiwala manyazi a ubwana wako, ndi citonzo ca umasiye wako sudzacikumbukiranso.