Isaiah 57:6 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Mumatenga miyala yosalala kumadamboko, ndi kumaipembedza ngati milungu. Mumapereka chopereka cha chakumwa kwa iyo, ndi kuperekanso chopereka cha chakudya. Kodi zimenezi zingandikondweretse?
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Pakuti pa miyala yosalala ya m'chigwa pali gawo lako; iyo ndiyo gawo lako; ndiyo imene unaitsanulirira nsembe yothira, ndi kupereka nsembe yaufa. Kodi ndidzapembedzedwa pa zinthu zimenezi?
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Mafano a pakati pa miyala yosalala ya mu zigwa ndiye chuma chanu. Inde, ndiye gawo lanu. Mumapereka chopereka cha chakumwa kwa mafanowo, ndipo mumaperekanso chopereka cha chakudya. Kodi zimenezi zingandichititse kuti ndikukomereni mtima?
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Pakuti pa miyala yosalala ya m'cigwa pali gawo lako; iyo ndiyo gawo lako; ndiyo imene unaitsanulirira nsembe yothira, ndi kupereka nsembe yaufa. Kodi ndidzapembedzedwa pa zinthu zimenezi?