Isaiah 58:4 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Mumati uku mukusala zakudya, uku mukukangana ndi kumenyana, mpaka kutchayana ndi nkhonya zopwetekana. Kodi mukuyesa kuti Ine nkumvera mapemphero anu, chifukwa cha kusala zakudya kotereku.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Taonani, inu musala kudya kuti mukangane ndi kutsutsana ndi kukantha ndi nkhonya yoipa; inu simusala kudya tsiku lalero kuti mumveketse mau anu kumwamba.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Mumati uku mukusala kudya, uku mukukangana ndi kumenyana, mpaka kumenyana ndi nkhonya zopweteka. Kusala kudya mukuchitiramu musayembekezere kuti mawu anu amveka kumwamba.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Taonani, inu musala kudya kuti mukangane ndi kutsutsana ndi kukantha ndi nkhonya yoipa; inu simusala kudya tsiku lalero kuti mumveketse mau anu kumwamba.