Isaiah 62:4 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Sudzatchedwanso “Wosiyidwa,” dziko lako silidzatchedwanso “Chipululu.” Dzina lako latsopanolo lidzakhala “Ndikukondwera naye.” Dziko lako lidzatchedwa “Wokwatiwa mwachimwemwe,” chifukwa choti Chauta akukondwera nawe, ndipo adzakhala ngati mwamuna wa dziko lako.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Iwe sudzatchedwanso Wosiyidwa; dziko lako silidzatchedwanso Bwinja; koma iwe udzatchedwa Hefiziba ndi dziko lako Beula; pakuti Yehova akondwera mwa iwe, ndipo dziko lako lidzakwatiwa.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Sadzakutchanso “Wosiyidwa,” ndipo dziko lako silidzatchedwanso “Chipululu.” Koma dzina lako latsopano lidzakhala “Ndakondwera naye.” Ndipo dziko lako lidzatchedwa “Wokwatiwa.” Chifukwa Yehova akukondwera nawe, ndipo adzakhala ngati mwamuna wa dziko lako.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Iwe sudzachedwanso Wosiyidwa; dziko lako silidzachedwanso Bwinja; koma iwe udzachedwa Hefiziba ndi dziko lako Beula; pakuti Yehova akondwera mwa iwe, ndipo dziko lako lidzakwatiwa.