Jeremiah 10:18 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Chauta akunena kuti, “Tsopano ndichotsa anthu onse a m'dziko lino. Ndidzaŵagwetsa m'mavuto, mpaka aŵamve ndithu.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Pakuti atero Yehova, Taonani, ndidzaponya kunja okhala m'dziko ili tsopanoli, ndi kuwasautsa, kuti azindikire.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Pakuti Yehova akuti, “Tsopano Ine ndidzachotsa anthu onse amene akukhala mʼdziko lino; adzakhala pa mavuto mpaka adzamvetsa.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Pakuti atero Yehova, Taonani, ndidzaponya kunja okhala m'dziko ili tsopanoli, ndi kuwasautsa, kuti azindikire.