Jeremiah 11:17 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Chauta Wamphamvuzonse, yemwe adakubzalani, ndiye wagamula kuti adzakulangani koopsa, chifukwa cha zoipa zimene mudachita, inu a m'banja la Israele ndi la Yuda. Mwamukwiyitsa pakupereka nsembe zopsereza kwa Baala.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Pakuti Yehova wa makamu, amene anakuoka iwe, wakunenera iwe choipa, chifukwa cha zoipa za nyumba ya Israele ndi nyumba ya Yuda, zimene anadzichitira okha pakuutsa mkwiyo wanga m'mene anafukizira Baala.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Yehova Wamphamvuzonse, amene anakudzalani, walamula kuti mavuto akugwereni. Inu a banja la Yuda ndi a banja la Israeli munachitira Yehova zoyipa ndi kumukwiyitsa pamene munkapereka nsembe zanu kwa Baala.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Pakuti Yehova wa makamu, amene anakuoka iwe, wakunenera iwe coipa, cifukwa ca zoipa za nyumba ya Israyeli ndi nyumba ya Yuda, zimene anadzicitira okha pakuutsa mkwiyo wanga m'mene anafukizira Baala.