Jeremiah 16:15 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Koma azidzati, ‘Pali Chauta wamoyo, amene adatulutsa Aisraele ku dziko lakumpoto, ndi ku maiko konse kumene adaŵabalalitsira!’ Ndithu ndidzaŵabwezera ku malo amene ndidapatsa makolo ao.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Koma, Pali Yehova, amene anakweza ana a Israele kuchokera kudziko la kumpoto, ndi kumaiko ena kumene anawapirikitsirako; ndipo ndidzawabwezanso kudziko lao limene ndinapatsa makolo ao.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
koma adzanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli ku dziko lakumpoto, ndi ku mayiko onse kumene anawabalalitsirako.’ Pakuti ndidzawabwezera ku dziko limene ndinalipereka kwa makolo awo.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Koma, Pali Yehova, amene anakweza ana a Israyeli kucokera ku dziko la kumpoto, ndi ku maiko ena kumene anawapitikitsirako; ndipo ndidzawabwezanso ku dziko lao limene ndinapatsa makolo ao.