Jeremiah 23:9 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Kunena za aneneri, mtima wanga wasweka, m'nkhongono mwachita kuti zii! Ndakhala ngati munthu woledzera, munthu wosokonezeka ndi vinyo, chifukwa cha Chauta ndi mau ake oyera.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Za aneneri. Mtima wanga usweka m'kati mwanga, mafupa anga onse anthunthumira; ndinga munthu woledzera, ngati munthu amene vinyo anamposa; chifukwa cha Yehova, ndi chifukwa cha mau ake opatulika.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Kunena za aneneri awa: Mtima wanga wasweka; mʼnkhongono mwati zii. Ndakhala ngati munthu woledzera, ngati munthu amene wasokonezeka ndi vinyo, chifukwa cha Yehova ndi mawu ake opatulika.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Za aneneri. Mtima wanga usweka m'kati mwanga, mafupa anga onse anthunthumira; ndinga munthu woledzera, ngati munthu amene vinyo anamposa; cifukwa ca Yehova, ndi cifukwa ca mau ace opatulika.