Jeremiah 31:10 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
“Mverani mau a Chauta, inu anthu a mitundu yonse. Mulalike mauwo ku maiko akutali a m'mbali mwa nyanja. Mulungu amene adabalalitsa Aisraele adzaŵasonkhanitsanso. Adzaŵasamala monga momwe mbusa amasamalira nkhosa zake.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Tamvani mau a Yehova, amitundu inu, lalikirani m'zisumbu zakutali; ndi kuti, Iye amene anabalalitsa Israele adzasonkhanitsa, nadzamsunga, monga mbusa achita ndi zoweta zake.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
“Imvani mawu a Yehova inu anthu a mitundu ina; lalikirani mawuwa kwa anthu a mayiko akutali a mʼmbali mwa nyanja; ‘Iye amene anabalalitsa Israeli adzawasonkhanitsanso ndipo adzayangʼanira nkhosa zake ngati mʼbusa.’
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Tamvani mau a Yehova, amitundu inu, lalikirani m'zisumbu zakutari; ndi kuti, Iye amene anabalalitsa Israyeli adzasonkhanitsa, nadzamsunga, monga mbusa acita ndi zoweta zace.