Jeremiah 51:46 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Musataye mtima. Musaope maphephe amene awanda m'dziko monse. Chaka ndi chaka pamabuka ndithu maphephe onena za nkhondo pa dziko lapansi, ndiponso zakuti mfumu yakutiyakuti ikumenyana ndi inzake.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Mtima wanu usalefuke, musaope chifukwa cha mbiri imene idzamveka m'dzikomu; pakuti mbiri idzafika chaka china, pambuyo pake chaka china mbiri ina, ndi chiwawa m'dziko, wolamulira kumenyana ndi wolamulira.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Musataye mtima kapena kuchita mantha pamene mphekesera zikumveka mʼdziko mwanu. Chaka ndi chaka pamabuka mphekesera za ziwawa mʼdziko lapansi, ndiponso yakuti mfumu yakuti ikuthira nkhondo mfumu ina.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Mtima wanu usalefuke, musaope cifukwa ca mbiri imene idzamveka m'dzikomu; pakuti mbiri idzafika caka cina, pambuyo pace caka cina mbiri yina, ndi ciwawa m'dziko, wolamulira kumenyana ndi wolamulira.