Jeremiah 6:10 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Kodi ndilankhule ndi yani, ndipo ndichenjeze yani, kuti amve? Makutu ao ndi otsekeka, sangathe kumva. Mau a Chauta amaŵanyoza kwambiri, saŵalabadira konse.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndidzanena ndi yani, ndidzachita mboni kwa yani, kuti amve? Taona khutu lao lili losadulidwa, ndipo sangathe kumva; taona, mau a Yehova awatonzetsa iwo; sakondwera nao.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Kodi ndiyankhule ndi yani ndi kumuchenjeza? Ndinene mawu ochenjeza kwa yani kuti amve? Makutu awo ndi otsekeka kotero kuti sangathe kumva. Mawu a Yehova ndi onyansa kwa iwo; sasangalatsidwa nawo.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndidzanena ndi yani, ndidzacita mboni kwa yani, kuti amve? Taona khutu lao liri losadulidwa, ndipo sangathe kumva; taona, mau a Yehova awatonzetsa iwo; sakondwera nao.